Maphunzitso a Mpinngo wosatsutsika?

“Zoonadi!

Bungwe akatswiri pa Chiphunzitso cha chikhulupiriro chathu lagamula kuti nkhani ya unsembe wa amayi ndi chiphunzitso chosasinthika!!!

a Kadinolo Ratzinger, Mtsogoleri wolamulira Bungwe la akatswiri pa za Malamulo woyera a Mpingo anati: ‘nkhani zokambirana unsembe wa amayi zamangika popeza nkhaniyi yalowa mu ziphunzitso zosatsuka za mpingo kudzera nchilamulo cha Aphunzitsi akulu a Mpingo. ”
Response to a Doubt, 28 October 1995

“Anaterodi? Kuletsa nkhayini, komadi?

A ‘Phunzitsi akulu a Mpingo a dziko lonse la pansi’ amayimira chiphunzitso ndi maganizo a ma Bishopi onse a Dziko la pansi.

Komano a Bishopi onse pamodzi sanagwirizanepo chiphunzitso chioletsa kupitiriza kukambirana unsembe wa Amayi.”

“Tayambani mwaima kaye!

Pali unyinji ma Bishopi a dziko la pansi omwe amakhulupirira kuti amayi sangadzodzedwe unsembe.

Izi nzachidziwikire chifukwa ambiri mwa ma Bishopiwa anasankhidwa chifukwa amagwirizana ndi maganizo a Papa pa nkhani ya unsembe wa Amayi!”

“Tiyeni tiunikirenso nkhaniyi!

Mkutheka kuti mabishopi onse a dziko la pansi amakhupirira kuti amayi siwoyenera kulowa unsembe. Chigwirizano choterechi chimaziwika ndi mau akuti opinio communis (maganizo ogwirizana).

Opinio communis Komano poyang’anira mbiri ya Mpingo tiona kuti chigwirizano cha maganizo a ma Bishopi chithanso kukhala ndi zolakwika.

Zaka 100 zapitazo ma bishopi ambiri amatsutsa maphunziro a Sayansi omwe amalongosola za mayambiriro a chilengedwe cha anthu. Nthawi imeneyo panali chikhupiriro chozama choti dziko linalenedwa m’masiku asanu ndi limodzi! Izi sizikutanthauza kuti ma Bishopi onse umagwirizana pa umphunzitsi umenewu.

“Nanga chimapangitsa kuti nkhani ikhale uphunzitsi wa ma Bishopi mogwirizana wogwizana ndi chiyani?

Kodi nsonkhano waukulu wachiri ku Vatikani sudagwirizana kuti: ‘Ma Bishopi, pamozdi ndi a Papa, monga a phunzitsi akulu mu Mpingo ayenera kulemekezedwa ndi aKhristu onse monga atetezi achifuniro cha Mulungu mu tchalitchi la Katolika?
Lumen Gentium § 25b.

“Chabwio, tiyeni tiwerengwe ndime yonse ya nkhaniyi!

Nsonkhano wachiwitri ku Vatikani udati: ‘ Ma Bishops angathe kulamula kuti maphunziro Khristu ndi wosatsutsika, nthawi ina iliyonse pomwe, ngakhale atakhala malo osasiyansiyana, pokhapokhapo ngati maganizo awo ngogwirizana ndi maganizo a Papa, ndipo maBishopi onsewa pamodzi ngati agwirizana kupereka uphunzitsi wowona pa za chikhulupiriro ndi umunthu. Ndipo payenera kukhala chigwirizano chopanda kukaika pa mfundo zomwe amanga limodzi. ’
Lumen Gentium § 25b.

Pali mfundo zisanu zoyeneretsa chigwirizanochi:

  1. Mgwirizano wa Bungwe la ma Bishopi.
    Mzachidzikire kuti ma Bishopi wonsewa ayenera kukhala wovomereka pa uphunzitsi wa za mpingo ngati gulu logwirizana.
  2. Monga ‘aweruzi’.
    Ma Bishopi ayenera kuperka maganizo awo a mumtima mwaufulu ndi mopanda mantha.
  3. Monga atumiki a Mpingo wonse.
    Ma Bishopiwa ayenera kumvvera mau a Mulungu womwe ‘Mzimu Woyera akuwauza mitima mwawo’.
  4. Mogwirizana ndi chikhulupiriro ndi malamulo.
    chiphunzitso choterechi chimayenera kupherezera mu mfundo za chikhulupiriro chathu.
  5. Kudzera mu chimphunzitso chomwe popanda kupeneka aganizira bwino kuti ndi ‘chiphunzitso choonadi.’
    Ndipo ma Bishopuwo mu mtima mwawo adziwe kuti ndi udindo wawo kutsutsa chiphunzitso chomwe chili ndi zopeneketsa.

Tikaunika pa nkhani ya unsembe wa amayi tiwona kuti nkhanii yatsekedwa mosatsatira dongosolo limeneli!

“Inu ma Bishopi mwavomereza magazizo ndi Kadinolo Ratzinger?!

Maganizo amenewa mwawatenga pa maphunzitso ati mu mpingo wathu?!”

“Akatswiri akuluakulu pa zophunzira za Mulungu akutsutsana ndi a Kadinolo Ratzinger pa zoletsa nkhani kupitiriza kukambirana nkhani ya unsembe wa amayi.
.

  1. Sukulu yaikulu ya maphunziro a unsembe ku Amereka
  2. Nicholas Lash, professor of divinity, Cambridge University, UK
  3. Francis A. Sullivan SJ, emeritus professor Gregorian University Rome
  4. Elizabeth A. Johnson, C.S.J., professor of theology at Fordham University, New York
  5. Gisbert Greshake, professor of theology at the University of Freiburg, Germany
  6. Ann O’Hara Graff, professor of theology at Seattle University, Washington
  7. Peter Hünermann, professor of theology at Tübingen University, Germany
  8. Sidney Cornelia Callahan, pastoral theologian, USA
  9. David Knight, pastoral theologian, Memphis, USA
  10. Richard Gaillardetz, associate professor, University of St. Thomas, Houseton, USA
  11. Klaus Nientiedt, ‘How Binding? “Ordinatio sacerdotalis” unleashes debate on the Magisterium’, Herder Korrespondenz 9 (1996) pp. 461-466.
  12. John H. Wright, ‘That all doubt may be removed’, America 171 (July 30-Aug. 6, 1994) pp. 16-19.
  13. Fr. Joseph Moingt SJ, editor of Recherches de Science Religieuse.
  14. Hugh O’Regan, editor of the on-line magazine, San Fransico Bay Catholic.
  15. The commission on “Woman and the Church” of the Belgian Bishops’ Conference

Mchifukwa chiyani tikutsutsana ndi uphunzitsi wa mpingo wa mtsankhoMafunso apafupipafupiZina?
kusintha kwa chikalidwemfundombirikumvera kwenikweninthumanzi ya chikhulupiriro
ufulu wokhala mayi?uphunzitsi wosatsutsika?kudalilika?kumvera?kederera?
Kodi ‘maufulu’ a aKatolika mtchalitchi ndi ati?
Muli ndi mafunso? __Maganizo ena? __Ndemanga?